Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 5:13-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pamenepo omveka otsala anatsika ndi anthu;Yehova ananditsikira pakati pa acamuna.

14. Anafika Aefraimu amene adika mizu m'Amaleki;Benjamini anakutsata iwe pakati pa anthu ako.Ku Makiri kudacokera olamulira,Ndi ku Zebuloni iwo akutenga ndodo ya mtsogoleri.

15. Akalonga a Isakara anali ndi Debora;Monga Isakara momwemo Baraki,Anawatuma m'cigwa namka coyenda pansi.Pa mitsinje ya Rubeni panali zotsimikiza mtima zazikuru.

16. Wakhaliranji pakati pa makola,Kumvera kulira kwa zoweta?Ku timitsinje ta Rubeni kunali zotsimikiza mtima zazikuru.

17. Gileadi anakhala tsidya lija la Yordano;Ndi Dani, akhaliranji mzombo?Aseri anakhala pansi m'mphepete mwa nyanja,Nakhalitsa pa nyondo yace ya nyanja.

18. Zebuloni ndiwo anthu anataya moyo wao mpaka imfa,Nafitali yemwe poponyana pamisanje.

19. Anadza mafumu, nathira nkhondoPamen'epo anathira nkhondo mafumu a Kanani.M'Taanaki, ku madzi a Megido;Osatengako phindu la ndarama.

20. Nyenyezi zinathira nkhondo yocokera kumwamba,M'mipita mwao zinathirana ndi Sisera.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 5