Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 5:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Inu akuyenda okwera pa aburu oyera,Inu akukhala poweruzira,Ndi inu akuyenda m'njira, fotokozerani.

11. Posamveka phokoso la amauta potunga madzi,Pomwepo adzafotokozera zolungama anazicita Yehova,Zolungama anazicita m'miraga yace, m'lsrayeli.Pamenepo anthu a Yehova anatsikira kuzipata.

12. Galamuka, Debora, galamuka,Galamuka, galamuka, unene nyimbo;Uka, Baraki, manga nsinga ndende zako, mwana wa Abinoamu, iwe.

13. Pamenepo omveka otsala anatsika ndi anthu;Yehova ananditsikira pakati pa acamuna.

14. Anafika Aefraimu amene adika mizu m'Amaleki;Benjamini anakutsata iwe pakati pa anthu ako.Ku Makiri kudacokera olamulira,Ndi ku Zebuloni iwo akutenga ndodo ya mtsogoleri.

15. Akalonga a Isakara anali ndi Debora;Monga Isakara momwemo Baraki,Anawatuma m'cigwa namka coyenda pansi.Pa mitsinje ya Rubeni panali zotsimikiza mtima zazikuru.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 5