Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 3:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo kunali, pakufika iye anaomba lipenga ku mapiri a Efraimu; ndi ana a Israyeli anatsika naye kucokera kumapiri, nawatsogolera iye.

28. Ndipo ananena nao, Nditsateni ine, pakuti Yehova wapereka adani anu Amoabu m'manja mwanu. Ndipo anatsika ndi kumtsata, natsekereza Amoabu madooko a Yordano, osalola mmodzi aoloke.

29. Ndipo anakantha Amoabu nyengo ija anthu zikwi khumi, onsewa anthu amoyo, ndi ngwazi; ndipo sanapulumuka ndi mmodzi yense.

30. Motero anagonjetsa Moabu tsiku lija pansi pa dzanja la Israyeli. Ndipo dziko linapumulazaka makumi asanu ndi atatu.

31. Atapita iye kunali Samagara, mwana wa Anati amene anakantha Afilisti mazana asanu ndi limodzi ndi mtoso wa ng'ombe; nayenso anapulumutsa Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 3