Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 3:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo iyo ndiyo mitundu ya anthu anaisiyapo Yehova kuyesa nayo Israyeli, ndiwo onse amene sanadziwa nkhondo zonse za Kanani;

2. cifukwa cace ndico cokha cakuti adziwitse mibadwo ya ana a Israyeli ndi kuwaphunzitsa nkhondo, ngakhale iwo okha okha osaidziwa konse kale;

3. anasiya mafumu asanu a Afilisti ndi Akanani onse, ndi Asidoni, ndi Ahivi okhala m'phiri la Lebano, kuyambira phiri la Baalaherimoni mpaka polowera ku Hamati.

4. Amenewo anakhala coyesera Israyeli kuti Yehova adziwe ngati adzamvere malamulo ace, amene analamulira makolo ao mwa dzanja la Mose.

5. Ndipo ana a Israyeli anakhala pakati pa Akanani, Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi;

6. nakwatira ana akazi a iwowa, napereka ana ao akazi kwa ana amuna a iwowa natumikira milungu yao.

7. Ndipo ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova, naiwala Yehova Mulungu wao, natumikira Abaala ndi zifanizo.

8. Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unayakira Israyeli ndipo anawagulitsa m'dzanja la KusaniRisataimu, mfumu ya Mesopotamiya; ndi ana a Israyeli anatumikira Kusani-Risataimu zaka zisanu ndi zitatu.

9. Ndipo pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova, Yehova anaukitsira ana a Israyeli mpulumutsi amene anawapulumutsa, ndiye Otiniyeli mwana wa'Kenazi, mng'ono wace wa Kalebe.

10. Ndipo unamdzera mzimu wa Yehova, iye naweruza Israyeli, naturuka kunkhondo; napereka Yehova Kusani-Risataimu mfumu ya Mesapotamiya m'dzanja lace; ndi dzanja lace linamlaka Kusani-Risataimu.

11. Pamenepo dziko linapumula zaka makumi anai; ndi Otiniveli mwana wa Kenazi anafa.

12. Koma ana a Israyeli anaonjezanso kucita coipa pamaso pa Yehova; pamenepo Yehova analimbitsa Egiloni mfumu ya Moabu pa Israyeli, popeza anacita coipa pamaso pa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 3