Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 21:23-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Nacita cotere ana a Benjamini, nadzitengera akazi monga mwa kuwerenga kwao, a obvina aja, amene anawatenga mwacifwamba; namuka iwo nabwerera ku colowa cao, namanga midzi, nakhalamo.

24. Ndipo ana a Israyeli anacokako nthawi ija yense kumka ku pfuko lace, ndi banja lace, naturukako yense kumka ku colowa cace.

25. Panalibe mfumu m'Israyeli masiku aja; a yense anacita comkomera pamaso pace.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 21