Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 16:4-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo pambuyo pace kunali kud anakonda mkazi m'cigwa ca Soreki, dzina lace ndiye Delila.

5. Ndipo akalonga a Atilisti anamkwerera mkaziyo, nanena naye, Umkope nuone umo mucokera mphamvu yace yaikuru, ndi umo tingakhoze kumtha khama, kuti timmange kumzunza; ndipo tidzakupatsa ali yense ndalama mazana khumi ndi limodzi.

6. Pamenepo Delila anati kwa Samsoni, Ndikupempha, undiuze umo mucokera mphamvu yako yaikuru, ndi cimene angakumange naco, kuti akuzunze.

7. Nanena naye Samsoni, Akandimanga nazo nsinga zatsopano zisanu ndi ziwiri zosauma, ndidzakhala wofoka, wakunga munthu wina.

8. Pamenepo akalonga a Afilisti anakwera nazo kwa mkaziyo nsinga zatsopano zisanu ndi ziwiri zosauma; ndipo iye anammanga nazo.

9. Koma anali nao omlalira m'cipinda ca m'kati. Nanena naye, Afilisti akugwera, Samsoni, Pamenepo anadula nsingazi, monga iduka nkhosi ya bwazi pokhudza moto. M'mwemo mphamvu yace siinadziwike.

10. Pamenepo Delila anati kwa Samsoni, Taona, wandipusitsa, ndi kundiuza mabodza; undiuze tsopano, ndikupempha, cimene angakumange naco.

11. Nanena naye, Akandimangitsa nazo zingwe zatsopano, zosagwira nazo nchito pamenepo ndidzakhala: wofoka wakunga munthu wina.

12. Ndipo Delila anatenga nsinga zatsopano, nammanga nazo, nanena naye, Atilisti akugwera, Samsoni. Ndi omlalira analikulinda m'cipinda ca m'kati. Koma anazidula pa manja ace ngati thonje.

13. Pamenepo Delila anati kwa Samsoni, Mpaka tsopano wandipusitsa, ndi kundiuza mabodza; undiuze cimene angakumange naco. Nanena naye, Ukaomba njombi zisanu ndi ziwiri za pamutu panga mwa thonje loyala ndiko.

14. Ndipo anacimanga ndi phanga, nati kwa iye, Akugwera Afilisti, Samsoni; nagalamuka iye patulo tace, nazula phanga la pamtanda, ndi thonje loyala lomwe.

15. Pamenepo ananena naye, Ukati bwanji, Ndikukonda, osamvana nane mtima wako? wandipusitsa katatu tsopano, osandiuza umo mucokera mphamvu yako yaikuru,

16. Ndipo kunali, popeza anamuumiriza masiku onse ndi mau ace, oamkakamiza, moyo wace unabvutika nkufuna kufa.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 16