Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 14:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo anatsika nakamba ndi mkazi, namkonda Samsoni pamaso pace.

8. Atapita masiku ndipo anabweranso kudzamtenga, napambuka iye kukaona mtembo wa mkango; ndipo taona, m'citanda ca mkango munali njuci zoundana, ndi uci.

9. Ndipo anaufula ndi dzanja lace, nayenda, namadya alimkuyenda, nadza kwa atate wace ndi amai wace, nawapatsa, nadya iwo; koma sanawauza kuti adaufula uciwo m'citanda ca mkango.

10. Ndipo atate wace anatsikira kwa mkazi; ndi Samsoni anakonzerapo madyerero; pakuti amatero anyamata.

11. Ndipo kunali, pamene anamuona, anabwera nao anzace makumi atatu akhale naye.

12. Nanena nao Samsoni, Mundilole ndikuphereni mwambi; mukanditanthauziratu uwu m'masiku asanuwa a madyerero, ndi kuukumika uwu, ndidzakupatsani malaya a nsaru yabafuta makumi atatu, ndi zobvala zosinthanitsa makumi atatu;

Werengani mutu wathunthu Oweruza 14