Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Samsoni anatsikira ku Timna, naona mkazi wa ku Timna wa ana akazi a Afilisti.

2. Nakwera iye, nauzaatatewacendi amai wace, nati, Ndapenya mkazi m'Timna wa ana akazi a Afilisti; ndipo tsono munditengere uyu akhale mkazi wanga.

3. Koma atate wace ndi amai wace ananena naye, Kodi palibe mkazi mwa ana akazi a abale ako, kapena mwa anthu a mtundu wanga onse, kuti wamuka kutenga mkazi wa Afilisti osadulidwawo? Nati Samsoni kwa atate wace, Nditengereni iye, pakuti andikonda pamaso panga.

4. Koma atate wace ndi amai wace sanadziwa kuti cidacokera kwa Yehova ici; popeza analikufuna kutola cifukwa ndi Afilisti. Ndipo nthawi ija Afilisti analamulira Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 14