Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 4:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mlongwanga, mkwatibwi ndiye munda wotsekedwa;Ngati kasupe wotsekedwa, ndi citsime copikiza.

13. Mphukira zako ndi munda wamakangaza,Ndi zipatso zofunika, bonongwe ndi mphoka,

14. Mphoka ndi cikasu,Nzimbe ndi ngaho, ndi mitengo yonse yamtanthanyerere;Nipa ndi khonje, ndi zonunkhiritsa zonse zomveka.

15. Ndiwe kasupe wa m'minda,Citsime ca madzi amoyo,Ndi mitsinje yoyenda yocokera ku Lebano.

16. Galamuka, mphepo ya kumpoto iwe, nudze, mphepo iwe ya kumwela;Nuombe pamunda panga, kuti zonunkhiritsa zace ziturukemo.Bwenzi langa mnyamatayo, alowe m'munda mwace,Nadye zipatso zace zofunika.

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 4