Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 1:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. NYIMBO yoposa, ndiyo ya Solomo.

2. Mnyamatayo andipsompsonetse ndi m'kamwa mwace;Pakuti cikondi cako ciposa vinyo.

3. Mafuta ako anunkhira bwino;Dzina lako likunga mafuta onunkhira otsanulidwa;Cifukwa cace anamwali akukonda.

4. Undikoke; tikuthamangire;Mfumu yandilowetsa m'zipinda zace:Tidzasangalala ndi kukondwera ndi iwe.Tidzachula cikondi cako koposa vinyo:Akukonda molungama.

5. Wakuda ine, koma wokongola,Ana akazinu a ku Yerusalemu,Ngati mahema a Kedara,Ngati nsaru zociriga za Solomo.

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 1