Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 7:52-66 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

52. tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

53. ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa za mphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Elisama mwana wa Amihudi.

54. Tsiku lacisanu ndi citatu kalonga wa ana a Manase ndiye Gamaliyeli mwana wa Pedazuri:

55. copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

56. cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

57. ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

58. tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

59. ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.

60. Tsiku lacisanu ndi cinai kalonga wa ana a Benjamini, ndiye Abidana mwana wa Gideoni:

61. copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

62. cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

63. ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

64. tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

65. ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Abidana mwana wa Gideoni.

66. Tsiku lakhumi kalonga wa ana a Dani, ndiye Ahiyezeri mwana wa Amisadai:

Werengani mutu wathunthu Numeri 7