Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 6:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Asadzidetse ndi atate wace, kapena mai wace, mbale wace, kapena mlongo wace, akafa iwowa; popeza cowindira Mulungu wace ciri pamutu pace.

8. Masiku onse a kusala kwace akhala wopatulikira kwa Yehova.

9. Munthu akafa cikomo pali iye, ndipo akadetsa mutu wace wowinda; pamenepo azimeta mutu wace tsiku la kumyeretsa kwace, tsiku lacisanu ndi ciwiri aumete.

Werengani mutu wathunthu Numeri 6