Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 4:42-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Ndipo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao,

43. kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu kuti agwire nchito m'cihema cokomanako,

44. owerengedwa ao monga mwa mabanja ao, ndiwo zikwi zitatu ndi mazana awiri.

45. Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.

46. Owerengedwa onse a Alevi, amene Mose ndi Aroni ndi akalonga a Israyeli anawawerengera, monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,

Werengani mutu wathunthu Numeri 4