Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 4:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Dati,

18. Musamasadza pfuko la mabanja a Kohati kuwacotsa pakati pa Alevi;

19. koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulikitsazo; Aroni ndi ana ace amuna alowe, namuikire munthu yense nchito yace ndi katundu wace.

20. Koma asalowe kukaona zopatulikazo pozikulunga, kuti angafe.

21. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

22. Werenganso ana a Gerisoni, monga mwa nyumba za makolo ao, monga mwa mabanja ao.

Werengani mutu wathunthu Numeri 4