16. Koma akamkantha ndi cipangizo cacitsulo, kuti wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.
17. Kapena akamkantha m'dzanja muli mwala, wakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.
18. Kapena akamkantha m'dzanja muli cipangizo camtengo, cakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.
19. Wolipsa mwazi mwini wace aphe wakupha munthuyo; pakumkumika amuphe,
20. Ndipo akampyoza momkwiyira, kapena kumponyera kanthu momlalira, kuti wafa;
21. kapena kumpanda ndi dzanja lace momuda, kuti wafa, womkanthayo nayenso amuphe ndithu; ndiye wakupha munthu; wolipsa mwazi aphe wakupha munthuyo pomkumika.
22. Koma akampyoza modzidzimuka, osamuda, kapena kumponyera kanthu osamialira,