Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 35:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo midziyo muipereke ikukhalireni midzi isanu ndi umodzi yopulumukirako.

14. Mupereke midzi itatu tsidya lino la Yordano, ndi midzi itatu mupereke m'dziko la Kanani, ndiyo yopulumukirako.

15. Midzi isanu ndi umodzi imene ndiyo yopulumukirako ana a Israyeli, ndi mlendo, ndi wokhala pakati pao; kuti ali yense adamupha munthu osati dala athawireko.

16. Koma akamkantha ndi cipangizo cacitsulo, kuti wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

17. Kapena akamkantha m'dzanja muli mwala, wakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

18. Kapena akamkantha m'dzanja muli cipangizo camtengo, cakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

19. Wolipsa mwazi mwini wace aphe wakupha munthuyo; pakumkumika amuphe,

Werengani mutu wathunthu Numeri 35