Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 35:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'zidikha za Moabu, pa Yordano, ku Yeriko, ndi kuti,

2. Uza ana a Israyeli, kuti apatseko Alevi colowa cao cao, midzi yokhalamo; muwapatsenso Alevi mabusa akuzungulira midzi.

3. Ndipo midzi ndiyo yokhalamo iwowa; ndi mabusa akhale a ng'ombe zao, ndi zoweta zao, inde nyama zao zonse.

4. Ndipo mabusa a midziyo, imene muipereke kwa Alevi ndiwo a mikono cikwi cimodzi kuyambira kulinga kufikira kunja.

Werengani mutu wathunthu Numeri 35