Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 33:40-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Ndipo Mkanani, mfumu ya Aradi, wakukhala kumwela m'dziko la Kanani, anamva za kudza kwao kwa ana a Israyeli.

41. Ndipo anacokera ku phiri la Hori, nayenda namanga m'Tsalimona.

42. Nacokera ku Tsalimona, nayenda namanga m'Punoni.

43. Nacokera ku Punoni, nayenda namanga m'Oboti.

44. Nacokera ku Oboti, nayenda namanga m'iye Abarimu, m'malire a Moabu.

45. Nacokera ku lyimu, nayenda namanga m'Diboni Gadi.

46. Nacokera ku Diboni Gadi, nayenda namanga m'Alimoni Diblataimu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 33