Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 32:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo anayandikiza, nati, Tidzamangira zoweta zathu makola kuno, ndi ana athu midzi; koma ife tidzakhala okonzeka ndi kufulumira pamaso pa ana a Israyeli, kufikira tidawafikitsa kumalo kwao;

17. ndi ang'ono athu adzakhala m'midzi ya malinga cifukwa ca okhala m'dzikomo.

18. Sitidzabwerera kwathu, kufikira ana a Israyeli atalandira yense colowa cace.

19. Pakuti sitidzalandira pamodzi nao tsidya la Yordano, ndi m'tsogolo mwace; popeza colowa cathu tacilandira tsidya lino la Yordano kum'mawa.

20. Ndipo Mose anati nao, Ngati mudzacita ici, ndi kudzikonza kunkhondo pamaso pa Yehova,

Werengani mutu wathunthu Numeri 32