Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 28:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Pamenepo muzipereka nsembe yopsereza ya pfungo lokoma kwa Yehova; ng'ombe zamphongo ziwiri, nkhosa yamphongo imodzi, ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi;

28. ndi nsembe yace ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe imodzi, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo imodzi,

29. limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi, momwemo ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;

30. tonde mmodzi wakutetezera inu.

31. Mupereke izi pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, zikhale kwa inu zopanda cirema, ndi nsembe zace zothira.

Werengani mutu wathunthu Numeri 28