52. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
53. Dziko ligawikire iwowa monga mwa kuwerenga kwa maina, likhale colowa cao.
54. Ocurukawo, uwacurukitsire colowa cao; ocepawo uwacepetsere colowa cao; ampatse yense colowa cace monga mwa owerengedwa ace.
55. Koma aligawe ndi kucita maere; colowa cao cikhale monga mwa maina a mafuko a makolo ao,
56. Agawire ocuruka ndi ocepa colowa cao monga mwa kucita maere.
57. Ndipo awa ndi owerengedwa ao a Alevi monga mwa mabanja ao: Gerisoni, ndiye kholo la banja la Agerisoni; Kohati, ndiye kholo la banja la Akohati; Merari, ndiye kholo la banja la Amerari.