Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 26:51-56 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

51. Iwo ndiwo owerengedwa ao a ana a Israyeli, zikwi mazana asanu ndi limodzi mphambu cimodzi kudza mazana asanu ndi awiri mphambu makumi atatu.

52. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

53. Dziko ligawikire iwowa monga mwa kuwerenga kwa maina, likhale colowa cao.

54. Ocurukawo, uwacurukitsire colowa cao; ocepawo uwacepetsere colowa cao; ampatse yense colowa cace monga mwa owerengedwa ace.

55. Koma aligawe ndi kucita maere; colowa cao cikhale monga mwa maina a mafuko a makolo ao,

56. Agawire ocuruka ndi ocepa colowa cao monga mwa kucita maere.

Werengani mutu wathunthu Numeri 26