Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 26:45-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Ana a Beriya ndiwo: Heberi, ndiye kholo la banja la Aheberi; Malikiyeli, ndiye kholo la banja la Amalikiyeli.

46. Ndipo dzina la mwana wamkazi wa Aseri ndiye Sera.

47. Iwo ndiwo mabanja a ana amuna a Aseri monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.

48. Ana amuna a Nafitali monga mwa mabanja ao ndiwo: Yazeli, ndiye kholo la banja la Ayazeli; Guni, ndiye kholo la banja la Aguni;

49. Yezeri, ndiye kholo la banja la Ayezeri; Silemu, ndiye kholo la banja la Asilemu.

50. Iwo ndiwo mabanja a Nafitali, monga mwa mabanja ao; ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana anai.

Werengani mutu wathunthu Numeri 26