Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 24:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndi Edomu adzakhala ace ace,Seiri lomwe lidzakhala lace lace, ndiwo adani ace;

19. Koma Israyeli adzacita zamphamvu.Ndipo wina woturuka m'Yakobo adzacita ufumu;Nadzapasula otsalira m'mudzi.

20. Ndipo anayang'ana ku Amaleki, nanena fanizo lace, nati,Amaleki ndiye woyamba wa amitundu;Koma citsiriziro cace, adzaonongeka ku nthawi zonse.

21. Ndipo anayang'ana Akeni, nanena fanizo lace, nati,Kwanu nkokhazikika,Wamanga cisa cako m'thanthwe.

22. Koma Kaini adzaonongeka,Kufikira Asuri adzakumanga nsinga.

23. Ndipo ananena fanizo lace, nati,Ha! adzakhala ndi moyo ndani pakucita ici Mulungu?

24. Koma zombo zidzafika kucokera ku doko la Kitimu,Ndipo adzasautsa Asuri, nadzasautsa Ebere,Koma iyenso adzaonongeka.

Werengani mutu wathunthu Numeri 24