14. Ndipo tsopano, taonani, ndimuka kwa anthu a mtundu wanga; tiyeni, ndidzakulangizani, ndi kukuuzani zimene anthu awa adzacitira anthu anu, masiku otsiriza.
15. Ndipo ananena fanizo lace, nati,Balamu mwana wa Beori anenetsa,Ndi munthu wotsinzina masoyo anenetsa;
16. Anenetsa wakumva mau a Mulungu,Ndi kudziwa nzeru ya Wam'mwambamwamba,Wakuona masomphenya a Wamphamvuyonse,Wakugwa pansi wopenyuka maso;
17. Ndimuona, koma tsopano ai; Ndimpenya, koma si pafupi ai;Idzaturuka nyenyezi m'Yakobo,Ndi ndodo yacifumu idzauka m'Israyeli,Nidzakantha malire a Moabu,Nidzapasula ana onse a Seti,