Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 24:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Balamu anaona kuti kudakomera pamaso pa Yehova kudalitsa Israyeli, sanamuka, monga nthawi zija zina, ku nyanga zolodzera, koma anayang'ana nkhope yace kucipululu.

2. Ndipo Balamu anakweza maso ace, naona Israyeli alikukhala monga mwa mafuko ao; ndipo mzimu wa Mulungu unadza pa iye.

3. Pamenepo ananena fanizo lace, nati,Balamu mwana wa Beori anenetsa,Ndi munthuyo anatsinzina maso anenetsa;

Werengani mutu wathunthu Numeri 24