Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 23:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Koma Balamu anayankha nati kwa Balaki, Sindinakuuzani ndi kuti, Ciri conse acinena Yehova, comweco ndizicita?

27. Ndipo Balaki anati kwa Balamu, Tiyetu, ndimuke nawe kumalo kwina; kapena kudzakomera pamaso pa Mulungu kuti unditembererere iwo pokhala kumeneko.

28. Ndipo Balaki anamka naye Balamu pamwamba pa Peori, popenyana ndi cipululu.

29. Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Mundimangire pano maguwa a nsembe asanu ndi awiri, nimundikonzere pano ng'ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri.

30. Ndipo Balaki anacita monga adanena Balamu, napereka ng'ombe ndi nkhosa yamphongo pa guwa la nsembe liri laose.

Werengani mutu wathunthu Numeri 23