Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 23:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Mulungu sindiye munthu, kuti aname;Kapena mwana wa munthu, kuti aleke;Kodi anena, osacita?

20. Kapena kulankhula, osacitsimikiza?Taonani, ndalandira mau akudalitsa,Popeza iye wadalitsa, sinditha kusintha.

21. Sayang'anira mphulupulu iri m'Yakobo,Kapena sapenya kupulukira kuli m'lsrayeli.Yehova Mulungu wace ali ndi iye,Ndi mpfuu wa mfumu uli pakati pao,

22. Mulungu awaturutsa m'Aigupto;Mphamvu yace ikunga ya njati.

Werengani mutu wathunthu Numeri 23