Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 23:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo anadza kuli iye, ndipo taona, analikuima pa nsembe yace yopsereza, ndi akalonga a Moabu pamodzi naye. Ndipo Balaki anati kwa iye, Wanenanji Yehova?

18. Ndipo ananena fanizo lace, nati,Ukani, Balaki, imvani;Ndimvereni, mwana wa Zipori;

19. Mulungu sindiye munthu, kuti aname;Kapena mwana wa munthu, kuti aleke;Kodi anena, osacita?

20. Kapena kulankhula, osacitsimikiza?Taonani, ndalandira mau akudalitsa,Popeza iye wadalitsa, sinditha kusintha.

21. Sayang'anira mphulupulu iri m'Yakobo,Kapena sapenya kupulukira kuli m'lsrayeli.Yehova Mulungu wace ali ndi iye,Ndi mpfuu wa mfumu uli pakati pao,

22. Mulungu awaturutsa m'Aigupto;Mphamvu yace ikunga ya njati.

23. Pakuti palibe nyanga pakati pa Yakobo,Kapena ula mwa Israyeli;Pa nyengo yace adzanena kwa Yakobo ndi Israyeli,Cimene Mulungu acita.

24. Taonani, anthuwo auka ngati mkango waukazi,Nadzitukumula ngati mkango waumuna:Sugonansokufikira utadya nyama yogwira,Utamwa mwazi wa zophedwa.

Werengani mutu wathunthu Numeri 23