15. Ndipo anati kwa Balaki, Imani pano pa nsembe yopsereza yanu, ndipite ine ndikakomane ndi iye uko.
16. Ndipo Yehova anakomana naye Balamu, naika mau m'kamwa mwace, nati, Bwerera kwa Balaki, nukanene cakuti cakuti.
17. Ndipo anadza kuli iye, ndipo taona, analikuima pa nsembe yace yopsereza, ndi akalonga a Moabu pamodzi naye. Ndipo Balaki anati kwa iye, Wanenanji Yehova?
18. Ndipo ananena fanizo lace, nati,Ukani, Balaki, imvani;Ndimvereni, mwana wa Zipori;
19. Mulungu sindiye munthu, kuti aname;Kapena mwana wa munthu, kuti aleke;Kodi anena, osacita?