Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 22:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pamenepo akalonga a Moabu ananyamuka, nafika kwa Balaki, nati, Alikukana Balamu kudza nafe.

15. Koma Balaki anaonjeza kutumanso akalonga, ocuruka, ndi omveka koposa awa.

16. Ndipo anadza kwa Balamu, nati kwa iye, Atero Balaki mwana wa Zipori, Pasakhaletu cinthu cakukuletsa kudza kwa ine;

17. popeza ndidzakucitira ulemu waukuru, ndipo zonse unena ndi ine ndidzacita; cifukwa cace idzatu, unditembererere anthu awa.

18. Ndipo Balamu, anayankha nati kwa anyamata a Balaki, Cinkana Balaki andipatsa nyumba yace yodzala ndi siliva ndi golidi, sindikhoza kutumpha mau a Yehova Mulungu wanga, kucepsako kapena kuonjezako.

Werengani mutu wathunthu Numeri 22