13. Ndipo Balamu anauka m'mawa, nati kwa akalonga a Balaki, Mukani ku dziko lanu; popeza Yehova andikaniza kuti ndisapite nanu,
14. Pamenepo akalonga a Moabu ananyamuka, nafika kwa Balaki, nati, Alikukana Balamu kudza nafe.
15. Koma Balaki anaonjeza kutumanso akalonga, ocuruka, ndi omveka koposa awa.
16. Ndipo anadza kwa Balamu, nati kwa iye, Atero Balaki mwana wa Zipori, Pasakhaletu cinthu cakukuletsa kudza kwa ine;