Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 2:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi asanu ndi awiri, mphambu zinai, kudza mazana asanu ndi limodzi.

5. Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Isakara; ndipo kalonga wa ana a Isakara ndiye Netandi mwana wa Zuwara.

6. Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zinai kudza mazana anai.

7. Ndi pfuko la Zebuloni: kalonga wa ana a Zebuloni ndiye Eliyabu mwana wa Heloni.

8. Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana anai.

9. Owerengedwa onse a cigono ca Yuda ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu ndi cimodzi mphambu mazana anai, monga mwa makamu ao, Ndiwo azitsogolera ulendo.

10. Mbendera ya cigono ca Rubeni ikhale kumwera monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Rubeni ndiye Elizuri mwana wa Sedeuri.

11. Ndi khamu lace, ndi olembedwa ace, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu ndi cimodzi kudza mazana asanu.

12. Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Simeoni; ndi kalonga wa ana a Simeoni ndiye Selumiyeli mwana wa Surisadai.

13. Ndi khamu lace ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi zinai kudza mazana atatu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 2