Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 2:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

2. Ana a Israyeli azimanga mahema ao yense ku mbendera yace, ya cizindikilo ca nyumba ya kholo lace; amange mahema ao popenyana ndi cihema cokomanako pozungulira.

3. Ndipo iwo akumanga mahema ao ku m'mawa koturuka dzuwa ndiwo a mbendera ya cigono ca Yuda, monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Yuda ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu.

4. Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi asanu ndi awiri, mphambu zinai, kudza mazana asanu ndi limodzi.

5. Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Isakara; ndipo kalonga wa ana a Isakara ndiye Netandi mwana wa Zuwara.

6. Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zinai kudza mazana anai.

7. Ndi pfuko la Zebuloni: kalonga wa ana a Zebuloni ndiye Eliyabu mwana wa Heloni.

8. Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana anai.

9. Owerengedwa onse a cigono ca Yuda ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu ndi cimodzi mphambu mazana anai, monga mwa makamu ao, Ndiwo azitsogolera ulendo.

10. Mbendera ya cigono ca Rubeni ikhale kumwera monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Rubeni ndiye Elizuri mwana wa Sedeuri.

Werengani mutu wathunthu Numeri 2