Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 16:30-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Koma Yehova akalenga cinthu catsopano, ndi nthaka ikayasama pakamwa pace, nikawameza ndi zonse ali nazo, nakatsikira iwo kumanda ali ndi moyo; pamenepo mudzadziwa kuti anthu awa anyoza Mulungu.

31. Ndipo kunali, pakutha iye kunena mau awa onse, nthaka inang'ambika pansi pao;

32. ndi dziko linayasama pakamwa pace ndi kuwameza, iwo ndi mabanja ao, ndi amuna ao onse akutsata Kora, ndi akatundu ao onse.

33. Comweco iwowa, ndi onse anali nao, anatsikira kumanda ali ndi moyo, ndi dziko linasunama pa iwo, ndipo anaonongeka pakati pa msonkhano.

34. Ndipo Aisrayeli onse akukhala pozinga pao anathawa pakumva kupfuula kwao; pakuti anati, Lingatimeze dziko ifenso.

35. Ndipo mota unaturuka kwa Yehova, ndi kunyeketsa amuna mazana awiri ndi makumi asanu aja akubwera naco cofukiza.

Werengani mutu wathunthu Numeri 16