Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 15:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Muzipatsa Yehova nsembe yokweza yoitenga ku mtanda wanu woyamba, mwa mibadwo yanu.

22. Ndipo pamene mulakwa, osacita mau awa onse amene Yehova ananena ndi Mose;

23. ndizo zonse Yehova anakuuzani ndi dzanja la Mose, kuyambira tsikulo Yehova anauza, ndi kunkabe m'mibadwo yanu;

24. pamenepo kudzali, ngati anacicita osati dala, osacidziwa khamulo, khamu lonse lipereke ng'ombe yamphongo ikhale nsembe yopsereza, ya pfungo lokoma ya Yehova, pamodzi ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira, monga mwa ciweruzo cace; ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo.

25. Ndipo wansembe azicita cotetezera khamu lonse la ana a Israyeli, ndipo adzakhululukidwa; popeza sanacita dala, ndipo anadza naco copereka cao, nsembe yamoto kwa Yehova, ndi nsembe yao yaucimo pamaso pa Yehova, cifukwa ca kulakwa osati dala.

26. Ndipo khamu lonse la ana a Israyeli, adzakhululukidwa, ndi mlendo yemwe wakukhala pakati pao; popeza khamu lonse linacicita osati dala.

27. Ndipo akacimwa munthu mmodzi osati dala, abwere nayo mbuzi yamsoti ya caka cimodzi, ikhale nsembe yaucimo.

Werengani mutu wathunthu Numeri 15