Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 15:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

18. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Pamene mulowa m'dziko limene ndirikukulowetsani,

19. kudzali, pakudya inu mkate wa m'dzikolo, muzikwezera Yehova nsembe yokweza.

20. Pa mtanda wanu woyamba muperekeko kamtanda, kakhale nsembe yokweza; monga mumacitira nsembe yokweza ya popuntha tirigu, momwemo muzikakweza.

21. Muzipatsa Yehova nsembe yokweza yoitenga ku mtanda wanu woyamba, mwa mibadwo yanu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 15