Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 14:39-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo Mose anauza ana a Israyeli mao onse awa; ndipo anthu anamva cisoni cambiri.

40. Ndipo anauka mamawa, nakwera pamwamba pa, phiri, nati, Tiri pano, tidzakwera kumka ku malo amene Yehova ananena; popeza tacimwa.

41. Ndipo Mose anati, Mutero cifukwa ninji kulakwira mau a Yehova, popeza simudzapindula nako?

42. Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

43. Pakuti Aamaleki ndi Akanani ali komweko patsogolo panu, ndipo mudzagwa ndi lupanga; popeza mwabwerera m'mbuyo osatsata Yehova, cifukwa cace Yehova sadzakhala nanu.

44. Koma anakwera pamwamba pa phiri modzikuza; koma likasa la cipangano la Yehova, ndi Mose, sanacoka kucigono.

45. Pamenepo anatsika Aamaleki, ndi Akanani, akukhala m'phirimo nawakantha, nawapha kufikira ku Horima.

Werengani mutu wathunthu Numeri 14