Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 14:38-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Koma Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebi mwana wa Yefune, anakhala ndi moyo mwa amuna aja adamukawo kukazonda dziko.

39. Ndipo Mose anauza ana a Israyeli mao onse awa; ndipo anthu anamva cisoni cambiri.

40. Ndipo anauka mamawa, nakwera pamwamba pa, phiri, nati, Tiri pano, tidzakwera kumka ku malo amene Yehova ananena; popeza tacimwa.

41. Ndipo Mose anati, Mutero cifukwa ninji kulakwira mau a Yehova, popeza simudzapindula nako?

42. Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 14