Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 14:34-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Monga mwa kuwerenga kwa masiku amene munazonda dziko, masiku makumi anai, tsiku limodzi kuwerenga caka cimodzi, mudzasenza mphulupulu zanu, zaka makumi anai, ndipo mudzadziwa kuti ndaleka lonjezano langa.

35. Ine Yehova ndanena, ndidzacitira ndithu ici khamu ili lonse loipa lakusonkhana kutsutsana nane; adzatha m'cipululu muno, nadzafamo.

36. Ndipo amunawo, amene Mose anawatumiza kukazonda dziko, amene anabwera nadandaulitsa khamu lonse pa iye, poipsa mbiri ya dziko,

37. amuna amene anaipsa mbiri ya dziko, anafa ndi mliri pamaso pa Yehova.

38. Koma Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebi mwana wa Yefune, anakhala ndi moyo mwa amuna aja adamukawo kukazonda dziko.

39. Ndipo Mose anauza ana a Israyeli mao onse awa; ndipo anthu anamva cisoni cambiri.

40. Ndipo anauka mamawa, nakwera pamwamba pa, phiri, nati, Tiri pano, tidzakwera kumka ku malo amene Yehova ananena; popeza tacimwa.

41. Ndipo Mose anati, Mutero cifukwa ninji kulakwira mau a Yehova, popeza simudzapindula nako?

42. Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

43. Pakuti Aamaleki ndi Akanani ali komweko patsogolo panu, ndipo mudzagwa ndi lupanga; popeza mwabwerera m'mbuyo osatsata Yehova, cifukwa cace Yehova sadzakhala nanu.

44. Koma anakwera pamwamba pa phiri modzikuza; koma likasa la cipangano la Yehova, ndi Mose, sanacoka kucigono.

Werengani mutu wathunthu Numeri 14