Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 13:7-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Wa pfuko la Isakara, Igali mwana wa Yosefe.

8. Wa pfuko la Efraimu, Hoseya mwana wa Nuni.

9. Wa pfuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu.

10. Wa pfuko la Zebuloni, Gadiyeli mwana wa Sodi.

11. Wa pfuko la Yosefe, wa pfuko la Manase, Gadi mwana wa Susi.

12. Wa pfuko la Dani, Amiyeli mwana wa Gemali.

13. Wa pfuko la Aseri, Setri mwana wa Mikayeli.

14. Wa pfuko la Nafitali, Nabi mwana wa Vopisi.

15. Wa pfuko la Gadi, Geyuelimwana wa Maki.

16. Awandi maina a amunawo Mose anawatumira azonde dziko. Ndipo Mose anamucha Hoseya mwana wa Nuni Yoswa.

17. Potero Mose anawatuma azonde dziko la Kanani, nanena nao, Kwerani uko kumwela, nimukwere kumapiri;

18. mukaone dziko umo liriri; ndi anthu akukhala m'mwemo, ngati ali amphamvu kapena ofok a, ngati acepa kapena acuruka;

19. ndi umo liriri dzikoli lokhalamo iwo, ngati lokoma, kapena loipa; ndi umo iriri midziyo akhalamo iwo, ngati akhala poyera kapena m'malinga;

Werengani mutu wathunthu Numeri 13