1. Ndipo Miriamu ndi Aroni anatsutsana naye Mose cifukwa ca mkazi mtundu wace Mkusi amene adamtenga; popeza adatenga mkazi Mkusi.
2. Ndipo anati, Kodi Yehova wanena ndi Mose yekha? sananenanso ndi ife nanga? Ndipo Yehova anamva.
3. Koma munthuyu Mose ndiye wofatsa woposa anthu onse a pa dziko lapansi.