Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 11:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. koma mwezi wamphumphu, kufikira ibwera m'mphuno mwako, ndi kuti ufukidwa nayo, pakuti mwakaniza Yehova wakukhala pakati pa inu, ndi kulira pamaso pace, ndi kuti, Tinaturukiranji m'Aigupto?

21. Ndipo Mose anati, Anthu amene ndiri pakati pao, ndiwo zikwi mazana asanu ndi limodzi oyenda pansi, ndipo Inu mwanena, Ndidzawapatsa nyama, kuti adye mwezi wamphumphu.

22. Kodi adzawaphera magulu a nkhosa ndi ng'ombe, kuwakwanira? kapena kodi nsomba zonse za m'nyanja zidzawasonkhanira pamodzi, kuwakwanira?

23. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kodi dzanja la Mulungu lafupikira? tsopano udzapenya ngati mau anga adzakucitikira kapena iai.

Werengani mutu wathunthu Numeri 11