Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 10:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Potero anayamba ulendo wao monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose.

14. Ndipo anayamba kuyenda a mbendera ya cigono ca ana a Yuda monga mwa magulu ao; woyang'anira gulu lace ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu.

15. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Isakara panali Netaneli mwana wa Zuwara.

16. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Zebuloni panali Eliyabu mwana wa Heloni.

17. Ndipo anagwetsa kacisi; ndi ana a Gerisoni, ndi ana a Merari, akunyamula kacisi, anamuka naye.

18. Ndi a mbendera ya cigono ca Rubeni, anayenda monga mwa magulu ao; ndipo pa gulu lace anayang'anira Elizuri mwana wa Sedeuri.

Werengani mutu wathunthu Numeri 10