Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 7:53-65 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

53. ana a Bakibuki, ana a Hakufa, ana a Harihuri,

54. ana a Baziliti, ana a Mehida, ana a Harisa,

55. ana a Barikosi, ana a Sisera, ana a Tema,

56. ana a Neziya, ana a Hatifa.

57. Ana a akapolo a Solomo: ana a Sotai, ana a Sofereti, ana a Perida,

58. ana a Yaala, ana a Darikoni, ana a Gideli,

59. ana a Sefatiya, ana a Hatili, ana a Pokereti Hazebaimu, ana a Amoni.

60. Anetini onse, ndi ana a akapolo a Solomo, ndiwo mazana atatu mphambu makumi asanu ndi anai kudza awiri.

61. Ndipo okwera kucokera ku Telemela, Teleharisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, ndi awa; koma sanakhoza kuchula nyumba za makolo ao, kapena mbumba zao, ngati ali a Israyeli;

62. ana a Delaya, ana a Tobiya, ana a Nekoda, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza awiri.

63. Ndi a ansembe: ana a Hobaya, ana a Hokozi, ana a Barizilai, amene anadzitengera mkazi wa ana akazi a Barizilai Mgileadi, nachedwa ndi dzina lao.

64. Awa anafunafuna maina ao m'buku la iwo owerengedwa mwa cibadwidwe, koma osawapeza; potero anawayesa odetsedwa, nawacotsa ku nchito ya nsembe.

65. Ndipo kazembe anawauza kuti asadyeko zopatulikitsa, mpaka wauka wansembe wokhala ndi Urimu ndi Tumimu.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 7