52. ana a Besai, ana a Meunimu, ana a Nefusesimu,
53. ana a Bakibuki, ana a Hakufa, ana a Harihuri,
54. ana a Baziliti, ana a Mehida, ana a Harisa,
55. ana a Barikosi, ana a Sisera, ana a Tema,
56. ana a Neziya, ana a Hatifa.
57. Ana a akapolo a Solomo: ana a Sotai, ana a Sofereti, ana a Perida,
58. ana a Yaala, ana a Darikoni, ana a Gideli,
59. ana a Sefatiya, ana a Hatili, ana a Pokereti Hazebaimu, ana a Amoni.
60. Anetini onse, ndi ana a akapolo a Solomo, ndiwo mazana atatu mphambu makumi asanu ndi anai kudza awiri.
61. Ndipo okwera kucokera ku Telemela, Teleharisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, ndi awa; koma sanakhoza kuchula nyumba za makolo ao, kapena mbumba zao, ngati ali a Israyeli;
62. ana a Delaya, ana a Tobiya, ana a Nekoda, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza awiri.
63. Ndi a ansembe: ana a Hobaya, ana a Hokozi, ana a Barizilai, amene anadzitengera mkazi wa ana akazi a Barizilai Mgileadi, nachedwa ndi dzina lao.
64. Awa anafunafuna maina ao m'buku la iwo owerengedwa mwa cibadwidwe, koma osawapeza; potero anawayesa odetsedwa, nawacotsa ku nchito ya nsembe.