25. Ana a Gibeoni, makumi asanu ndi anai kudza asanu.
26. Amuna a ku Betelehemu ndi ku Netofa, zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza asanu ndi atatu.
27. Amuna a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
28. Amuna a ku Bete-Azimaveti, makumi anai kudza awiri.
29. Amuna a ku Kiriyati Yearimu, Kefiira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.
30. Amuna a ku Rama ndi Geba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
31. Amuna a ku Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.
32. Amuna a ku Betele ndi Ai, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.
33. Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.
34. Ana a Elamu winayo, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.
35. Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.
36. Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.
37. Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
38. Ana a Senaa, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi anai kudza makumi atatu.
39. Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.
40. Ana a Imeri, cikwi cimodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.
41. Ana a Pasuru, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi anai ndi asanu ndi awiri.