19. Ana a Bigivai, zikwi ziwiri mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi awiri.
20. Ana a Adini, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza asanu.
21. Ana a Aberi, a Hezekiya, makumi asanu ndi anai kudza asanu ndi atatu.
22. Ana a Hasumu, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
23. Ana a Bezai, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza anai.
24. Ana a Harifi, zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.
25. Ana a Gibeoni, makumi asanu ndi anai kudza asanu.
26. Amuna a ku Betelehemu ndi ku Netofa, zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza asanu ndi atatu.
27. Amuna a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
28. Amuna a ku Bete-Azimaveti, makumi anai kudza awiri.
29. Amuna a ku Kiriyati Yearimu, Kefiira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.
30. Amuna a ku Rama ndi Geba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
31. Amuna a ku Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.
32. Amuna a ku Betele ndi Ai, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.
33. Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.