Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 3:29-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Potsatizana nao anakonza Zadoki mwana wa Imeri pandunji pa nyumba yace. Ndi potsatizana naye anakonza Semaya mwana wa Sekaniya, wosunga cipata ca kum'mawa.

30. Potsatizana naye Hananiya mwana wa Selemiya, ndi Hanuni mwana wacisanu ndi cimodzi wa Salafi, anakonza gawo lina. Potsatizana naye anakonza Mesulamu mwana wa Berekiya pandunji pa cipinda cace.

31. Potsatizana naye anakonza Malikiya wina wa osula golidi kufikira ku nyumba ya Anetini, ndi ya ocita malonda, pandunji pa cipata ca Hamifikadi, ndi ku cipinda cosanja ca kungondya.

32. Ndi pakati pa cipinda cosanja ca kungondya ndi cipata cankhosa anakonza osula golidi ndi ocita malonda.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 3