Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 3:21-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Potsatizana naye Meremoti mwana wa Uliya mwana wa Hakozi anakonza gawo lina, kuyambira ku khomo la nyumba ya Eliasibu kufikira malekezero ace a nyumba ya Eliasibu.

22. Ndi potsatizana naye anakonza ansembe okhala kucidikha.

23. Potsatizana nao anakonza Benjamini ndi Hasubi pandunji pa nyumba pao, Potsatizana nao anakonza Azariya mwana wa Maseya mwana wa Ananiya pafupi pa nyumba yace.

24. Potsatizana naye Binui mwana wa Henadadi anakonza gawo lina, kuyambira ku nyumba ya Azariya kufikira popindirira kufikira kungondya.

25. Palali mwana wa Uzai anakonza pandunji popindirira, ndi nsanja yosomphoka pa nyumba ya mfumu ya kumtunda, imene iri ku bwalo la kaidi. Potsatizana naye anakonza Pedaya mwana wa Parosi.

26. Koma Anetini okhala m'Ofeli anakonza kufikira ku malo a pandunji pa cipata ca kumadzi kum'mawa, ndi nsanja yosomphokayo,

27. Potsatizana nao Atekoa anakonza gawo lina, pandunji pa nsanja yaikuru yosomphoka ndi ku linga la Ofeli.

28. Kumtunda kwa cipata ca akavalo anakonza ansembe, yense pandunji pa nyumba yace.

29. Potsatizana nao anakonza Zadoki mwana wa Imeri pandunji pa nyumba yace. Ndi potsatizana naye anakonza Semaya mwana wa Sekaniya, wosunga cipata ca kum'mawa.

30. Potsatizana naye Hananiya mwana wa Selemiya, ndi Hanuni mwana wacisanu ndi cimodzi wa Salafi, anakonza gawo lina. Potsatizana naye anakonza Mesulamu mwana wa Berekiya pandunji pa cipinda cace.

31. Potsatizana naye anakonza Malikiya wina wa osula golidi kufikira ku nyumba ya Anetini, ndi ya ocita malonda, pandunji pa cipata ca Hamifikadi, ndi ku cipinda cosanja ca kungondya.

32. Ndi pakati pa cipinda cosanja ca kungondya ndi cipata cankhosa anakonza osula golidi ndi ocita malonda.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 3